Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 10:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2. Dzipangire malipenga awiri asiliva; uwasule mapangidwe ace; ucite nao poitana khamu, ndi poyendetsa a m'zigono.

3. Akaliza, khamu lonse lisonkhane kuli iwe ku khomo la cihema cokomanako,

4. Akaliza limodzi, pamenepo akalonga, akuru a zikwi a m'Israyeli, azisonkhana kuli iwe.

5. Mukaliza cokweza, ayende a m'zigono za kum'mawa.

6. Mukalizanso cokweza, a m'zigono za kumwela ayende; alize cokweza pakumuka.

7. Pomemeza msonkhano mulize, wosati cokweza ai.

8. Ana amuna a Aroni, ansembe, ndiwo aziliza malipenga; ndipo akhale kwa inu lemba losatha ku mibadwo yanu.

9. Ndipo pamene mupita kunkhondo m'dziko lanu kucita nkhondo pa mdani wakusautsa inu, mulize cokweza ndi malipenga; ndipo Yehova Mulungu wanu adzakumbukila inu, nadzakupulumutsani kwa adani anu.

10. Momwemo tsiku lakukondwera inu, ndi nyengo zoikidwa zanu, ndi poyamba miyezi yanu, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza, ndi pa nsembe zanu zoyamika; ndipo akhale kwa inu cikumbutso pamaso pa Mulungu wanu; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

Werengani mutu wathunthu Numeri 10