Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 9:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo munapenya msauko wa makolo athu m'Aigupto, nimunamva kupfuula kwao ku Nyanja Yofiira,

10. nimunacitira zizindikilo ndi zodabwiza Farao ndi akapolo ace onse, ndi anthu onse a m'dziko lace; popeza munadziwa kuti anawacitira modzikuza; ndipo munadzibukitsira dzina monga lero lino.

11. Ndipo munagawanitsa nyanja pamaso pao, napita iwo pakati pa nyanja pouma, ndipo munaponya mozama owalondola, ngati mwala m'madzi olimba.

12. Munawatsogoleranso usana ndi mtambo woti njo, ndi moto tolo usiku, kuwaunikira m'njira akayendamo.

13. Munatsikiranso pa phiri la Sinai, nimunalankhula nao mocokera m'Mwamba, ndipo munawapatsa maweruzo oyenera, ndi cilamulo coona, malemba, ndi malamulo okoma;

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 9