Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 9:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo tsiku la makumi awiri mphambu anai la mwezi uno ana a Israyeli anasonkhana ndi kusala, ndi kubvala ciguduli, ndipo anali ndi pfumbi.

2. Nadzipatula a mbumba ya Israyeli kwa alendo onse, naimirira, naulula zocimwa zao, ndi mphulupulu za makolo ao.

3. Naimima poima pao, nawerenga m'buku la cilamulo ca Yehova Mulungu wao limodzi la magawo anai a tsiku; ndi limodzi la magawo anai anaulula, napembedza Yehova Mulungu wao.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 9