Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 8:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo Alevi anatontholetsa anthu onse, ndi kuti, Khalani muli cete; pakuti lero ndi lopatulika; musamacita cisoni.

12. Napita anthu onse kudya ndi kumwa, ndi kutumiza magawo, ndi kusekerera kwakukuru; popeza anazindikira mau amene adawafotokozera.

13. Ndipo m'mawa mwace akuru a nyumba za makolo a anthu onse, ansembe, ndi Alevi anasonkhana pamodzi kwa Ezara mlembi, kuti atole nzeru za mau a cilamulo.

14. Napeza munalembedwa m'cilamulo kuti Yehova analamulira ndi Mose, kuti ana a Israyeli azikhala m'misasa pa madyerero a mwezi wacisanu ndi ciwiri,

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 8