Ndi cipata ca kukasupe anacikonza Saluni mwana wa Koli, Hoze mkuru wa dziko la Mizipa anacimanga, nacikomaniza pamwamba pace, naika zitseko zace, zokowera zace, ndi mipiringidzo yace; ndiponso linga la dziwe la Sela pa munda wa mfumu, ndi kufikira ku makwerero otsikira ku mudzi wa Davide.