Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 2:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Atamva Sanibalati Mhoroni, ndi Tobiya kapoloyo M-amoni, cidawaipira kwakukuru, kuti wadza munthu kuwafunica ana a Israyeli cokoma.

11. Motero ndinafika ku Yerusalemu, ndi kukhalako masiku atatu.

12. Ndipo ndinauka usiku, ine ndi amuna owerengeka nane, osauza munthu yense ine coika Mulungu wanga m'mtima mwanga ndicitire Yerusalemu; panalibenso nyama yina nane, koma nyama imene ndinakhalapo.

13. Ndipo ndinaturuka usiku pa cipata ca kucigwa, kumka ku citsime ca cinjoka, ndi ku cipata ca kudzala, ndi kuyang'ana malinga a Yerusalemu adapasukawo, ndi zipata zace zothedwa ndi moto.

14. Ndipo ndinapitima kumka ku cipata cacitsime, ndi ku dziwe la mfumu; koma popita nyama iri pansi panga panaicepera.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 2