Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 9:7-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Tiye, idya zakudya zako mokondwa, numwe vinyo wako mosekera mtima; pakuti Mulungu wabvomerezeratu zocita zako.

8. Zobvala zako zikhale zoyera masiku onse; mutu wako usasowe mafuta.

9. Khalani mokondwa ndi mkazi umkonda masiku onse a moyo wako wacabe, umene Mulungu wakupatsa pansi pano masiku ako onse acabe; pakuti ilo ndi gawo lako la m'moyo ndi m'nchito zimene ubvutika nazo pansi pano.

10. Ciri conse dzanja lako licipeza kucicita, ucicite ndi mphamvu yako; pakuti mulibe nchito ngakhale kulingirira ngakhale kudziwa, ngakhale nzeru, kumanda ulikupitako.

11. Ndinabweranso ndi kuzindikira pansi pano kuti omwe atamanga msanga sapambana m'liwiro, ngakhale olimba sapambana m'nkhondo, ngakhale anzeru sapeza zakudya, ngakhale ozindikira bwino salemera, ngakhale odziwitsa sawakomera mtima; koma yense angoona zomgwera m'nthawi mwace.

12. Pakuti munthu sadziwatu mphindi yace; monga nsomba zigwidwa m'ukonde woipa, ndi mbalame zikodwa mumsampha, momwemo ana a anthu amagwidwa ndi nthawi ya tsoka, ngati msampha umene uwagwera modzidzimuka.

13. Ndaonanso nzeru pansi pano motero, ndipo inandionekera yaikuru;

14. panali mudzi waung'ono muli anthu owerengeka; ndipo inadzako mfumu yaikuru, niizinga ndi nkhondo, nimangapo malinga akuru;

15. koma anapezedwamo mwamuna wanzeru wosauka, yemweyo napulumutsa mudziwo ndi nzeru yace; koma panalibe anthu anakumbukira wosauka ameneyo.

16. Pamenepo ndinati, Nzeru ipambana mphamvu; koma anyoza nzeru ya wosauka, osamvera mau ace.

17. Mau a anzeru acete amveka koposa kupfuula kwa wolamulira mwa zitsiru.

18. Nzeru ipambana zida za nkhondo; koma wocimwa mmodzi aononga zabwino zambiri.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 9