Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 9:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Cikondi cao ndi mdano wao ndi dumbo lao lomwe zatha tsopano; ndipo nthawi yamuyaya sagawa konse kanthu kali konse kacitidwa pansi pano.

7. Tiye, idya zakudya zako mokondwa, numwe vinyo wako mosekera mtima; pakuti Mulungu wabvomerezeratu zocita zako.

8. Zobvala zako zikhale zoyera masiku onse; mutu wako usasowe mafuta.

9. Khalani mokondwa ndi mkazi umkonda masiku onse a moyo wako wacabe, umene Mulungu wakupatsa pansi pano masiku ako onse acabe; pakuti ilo ndi gawo lako la m'moyo ndi m'nchito zimene ubvutika nazo pansi pano.

10. Ciri conse dzanja lako licipeza kucicita, ucicite ndi mphamvu yako; pakuti mulibe nchito ngakhale kulingirira ngakhale kudziwa, ngakhale nzeru, kumanda ulikupitako.

11. Ndinabweranso ndi kuzindikira pansi pano kuti omwe atamanga msanga sapambana m'liwiro, ngakhale olimba sapambana m'nkhondo, ngakhale anzeru sapeza zakudya, ngakhale ozindikira bwino salemera, ngakhale odziwitsa sawakomera mtima; koma yense angoona zomgwera m'nthawi mwace.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 9