Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 6:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Nchito zace zonse munthu angogwirira m'kamwa mwace, koma mtima wace sukhuta.

8. Pakuti wanzeru ali ndi ciani coposa citsiru? Waumphawi wodziwa kuyenda pa maso pa amoyo ali ndi ciani?

9. Kupenya kwa maso kuposa kukhumba kwa mtima; icinso ndi cabe ndi kungosautsa mtima.

10. Comwe cinalipo cachedwa dzina lace kale, cidziwika kuti ndiye munthu; sakhoza kulimbana ndi womposa mphamvu.

11. Pokhala zinthu zambiri zingocurukitsa zacabe, kodi anthu aona phindu lanji?

12. Pakuti ndani adziwa comwe ciri cabwino kwa munthu ali ndi moyo masiku onse a moyo wace wacabe umene autsiriza ngati mthunzi? pakuti ndani adzauza munthu cimene cidzaoneka m'tsogolo mwace kunja kuno?

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 6