Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 5:3-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Pakuti loto lafika mwakucuruka nchito; ndipo mau a citsiru mwakucuruka maneno.

4. Utawinda ciwindo kwa Mulungu, usacedwe kucicita; pakuti sakondwera ndi zitsiru; cita comwe unaciwindaco.

5. Kusawinda kupambana kuwinda osacita,

6. Usalole m'kamwa mwako mucimwitse thupi lako; usanene pamaso pa mthenga kuti, Ndinaphophonya; Mulungu akwiyire mau ako cifukwa ninji, naononge nchito ya manja ako?

7. Pakuti monga mu unyinji wa maloto muli zacabe motero mocuruka mau; koma dziopa Mulungu.

8. Ukaona anthu alikutsendereza aumphawi, ndi kucotsa cilungamo ndi ciweruzo mwaciwawa pa dera lina la dziko, usazizwepo; pakuti mkuru wopambana asamalira; ndipo alipo akuru ena oposa amenewo.

9. Phindutu la dziko lipindulira onse; ngakhale mfumu munda umthandiza.

10. Wokonda siliva sadzakhuta siliva; ngakhale wokonda cuma sadzakhuta phindu; icinso ndi cabe.

11. Pocuruka katundu, akudyapo acurukanso; nanga apindulira eni ace ciani, koma kungopenyera ndi maso ao?

12. Tulo ta munthu wogwira nchito ntabwino, ngakhale adya pang'ono ngakhale zambiri; koma kukhuta kwa wolemera sikumgonetsa tulo.

13. Pali coipa cobvuta ndaciona kunja kuno, ndico, cuma cirikupweteka eni ace pocikundika;

14. koma cumaco cionongeka pomgwera tsoka; ndipo akabala mwana, m'dzanja lace mulibe kanthu.

15. Monga anaturuka m'mimba ya amace, adzabweranso kupita wamarisece, monga anadza osatenga kanthu pa nchito zace, kakunyamula m'dzanja lace.

16. Icinso ndi coipa cowawa, cakuti adzangopita monse monga anadza; ndipo wodzisautsa cabe adzaona phindu lanji?

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 5