Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 2:21-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Pakuti pali munthu wina agwira nchito mwanzeru ndi modziwa nadzipinduliramo; koma adzapereka gawo lace kwa munthu amene sanagwirapo nchito. Icinso ndi cabe ndi coipa cacikuru.

22. Pakuti munthu ali ndi ciani m'nchito zace zonse, ndi m'kusauka kwa mtima wace amasauka nazozo kunja kuno?

23. Pakuti masiku ace onse ndi zisoni, bvuto lace ndi kumliritsa; ngakhale usiku mtima wace supuma. Icinso ndi cabe.

24. Kodi si cabwino kuti munthu adye namwe, naonetse moyo wace, zabwino m'nchito yace? icinso ndinacizindikira kuti cicokera ku dzanja la Mulungu.

25. Pakuti ndani angadye ndi kufulumirako, koposa ine.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 2