Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mika 7:18-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndani Mulungu wofanana ndi Inu, wakukhululukira mphulupulu, wakupitirira zolakwa za otsala a colowa cace? sasunga mkwiyo wace ku nthawi yonse popeza akondwera naco cifundo.

19. Adzabwera, nadzaticitira nsoni; adzagonjetsa mphulupulu zathu; ndipo mudzataya zocimwa zao zonse m'nyanja yakuya,

20. Mudzapatsa kwa Yakobo coonadi, ndi kwa Abrahamu cifundo cimene munalumbirira makolo athu kuyambira masiku a kale lomwe.

Werengani mutu wathunthu Mika 7