11. Ndipo tsopano amitundu ambiri asonkhana kuyambana nawe, akuti, Aipsidwe, diso lathu lipenye ku Ziyoni.
12. Koma sadziwa zolingirira za Yehova, kapena kuzindikira uphungu wace; pakuti anawasonkhanitsa ngati mitolo kudwale.
13. Nyamuka nupunthe, mwana wamkazi wa Ziyoni; pakuti ndidzasanduliza nyanga yako ikhale yacitsulo, ndi ziboda zako zikhale zamkuwa; ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu; ndipo uzipereka ciperekere phindu lao kwa Yehova, ndi cuma cao kwa Ambuye wa dziko lonse lapansi.