Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mika 4:11-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo tsopano amitundu ambiri asonkhana kuyambana nawe, akuti, Aipsidwe, diso lathu lipenye ku Ziyoni.

12. Koma sadziwa zolingirira za Yehova, kapena kuzindikira uphungu wace; pakuti anawasonkhanitsa ngati mitolo kudwale.

13. Nyamuka nupunthe, mwana wamkazi wa Ziyoni; pakuti ndidzasanduliza nyanga yako ikhale yacitsulo, ndi ziboda zako zikhale zamkuwa; ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu; ndipo uzipereka ciperekere phindu lao kwa Yehova, ndi cuma cao kwa Ambuye wa dziko lonse lapansi.

Werengani mutu wathunthu Mika 4