4. Pakuti pamaso panu zaka zikwiZikhala ngati dzulo, litapita,Ndi monga ulonda wa usiku.
5. Muwatenga ngati ndi madzi akulu, akhala ngati tulo;Mamawa akhala ngati msipu waphuka.
6. Mamawa uphuka bwino;Madzulo ausenga, nuuma.
7. Pakuti tionongeka mu mkwiyo wanu;Ndipo m'kuzaza kwanu tiopsedwa.
8. Munaika mphulupulu zathu pamaso panu,Ndi zoipa zathu zobisika pounikira nkhope yanu.
9. Pakuti masiku athu onse apitirira m'ukali wanu;Titsiriza moyo wathu ngati lingaliro.
10. Masiku a zaka zathu ndiwo zaka makumi asanu ndi awiri,Kapena tikakhala nayo mphamvudi zaka makumi asanu ndi atatu;Koma teronso kukula kwao kumati cibvuto ndi copanda pace;Pakuti kumapitako msanga ndipo tithawa ife tomwe.
11. Adziwa mphamvu ya mkwiyo wanu ndani,Ndi ukali wanu monga ayenera kukuopani?
12. Mutidziwitse kuwerenga masiku athu motero,Kuti tikhale nao mtima wanzeru.