Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 90:3-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Mubweza munthu akhale pfumbi;Nimuti, Bwererani inu, ana a anthu.

4. Pakuti pamaso panu zaka zikwiZikhala ngati dzulo, litapita,Ndi monga ulonda wa usiku.

5. Muwatenga ngati ndi madzi akulu, akhala ngati tulo;Mamawa akhala ngati msipu waphuka.

6. Mamawa uphuka bwino;Madzulo ausenga, nuuma.

7. Pakuti tionongeka mu mkwiyo wanu;Ndipo m'kuzaza kwanu tiopsedwa.

8. Munaika mphulupulu zathu pamaso panu,Ndi zoipa zathu zobisika pounikira nkhope yanu.

9. Pakuti masiku athu onse apitirira m'ukali wanu;Titsiriza moyo wathu ngati lingaliro.

10. Masiku a zaka zathu ndiwo zaka makumi asanu ndi awiri,Kapena tikakhala nayo mphamvudi zaka makumi asanu ndi atatu;Koma teronso kukula kwao kumati cibvuto ndi copanda pace;Pakuti kumapitako msanga ndipo tithawa ife tomwe.

11. Adziwa mphamvu ya mkwiyo wanu ndani,Ndi ukali wanu monga ayenera kukuopani?

Werengani mutu wathunthu Masalmo 90