Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 64:3-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Amene anola lilime lao ngati lupanga,Napiringidza mibvi yao, ndiyo mau akuwawitsa;

4. Kuponyera wangwiro mobisika:Amponyera modzidzimutsa, osaopa.

5. Alimbikitsana m'cinthu coipa;Apangana za kuchera misampha mobisika;Akuti, Adzaiona ndani?

6. Afunafuna zosalungama; kusanthula, asanthuladi kutha;Cingakhale ca m'kati mwace mwa munthu, ndi mtima wozama.

7. Koma Mulungu adzawaponyera mubvi;Adzalaswa modzidzimutsa,

8. Adzawakhumudwitsa, lilime lao lidzawatsutsa;Onse akuwaona adzawathawa.

9. Ndipo anthu onse adzacita mantha;Nadzabukitsa cocita Mulungu,Nadzasamalira nchito yace.

10. Wolungama adzakondwera mwa Yehova, nadzakhulupirira Iye;Ndipo oongoka mtima onse adzalemekeza.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 64