1. Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu,Ndipo musandilange m'ukali wanu.
2. Mundicitire cifundo, Yehova; pakuti ndalefuka ine:Mundicize, Yehova; pakuti anthunthumira mafupa anga.
3. Moyo wanganso wanthunthumira kwakukuru;Ndipo Inu, Yehova, kufikira liti?
4. Bwererani Yehova, landitsani moyo wanga;Ndipulumutseni cifukwa ca kukoma mtima kwanu.
5. Pakuti muimfa m'mosakumbukila Inu:M'mandamo adzakuyamikani dani?