Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 51:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mundicitire ine cifundo, Mulungu,Monga mwa kukoma mtima kwanu;Monga mwa unyinji wa nsoni zokoma zanuMufafanize macimo anga.

2. Mubwereze kunditsuka mphulupulu yanga,Ndipo mundiyeretse kundicotsera coipa canga,

3. Cifukwa ndazindikira macimo anga;Ndipo coipa canga ciri pamaso panga cikhalire:

4. Pa Inu, Inu nokha, ndinacimwa,Ndipo ndinacicita coipaco pamaso panu:Kuti mukhale wolungama pakulankhula Inu,Mukhalenso woyera pa kuweruza kwanu.

5. Onani, ndinabadwa m'mphulupulu:Ndipo mai wanga anandilandira m'zoipa.

6. Onani, Inu mukondwera ndi zoonadi m'malo a m'katimo;Ndipo m'malo a m'tseri mudzandidziwitsa nzeru.

7. Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera;Munditsuke ndipo ndidzakhala wa mbu woposa matalala.

8. Mundimvetse cimwemwe ndi kusekera:Kuti mafupawo munawatyola akondwere.

9. Muzibisire nkhope yanu zolakwa zanga,Ndipo mufafanize mphulupulu zanga zonse.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 51