Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 51:1-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mundicitire ine cifundo, Mulungu,Monga mwa kukoma mtima kwanu;Monga mwa unyinji wa nsoni zokoma zanuMufafanize macimo anga.

2. Mubwereze kunditsuka mphulupulu yanga,Ndipo mundiyeretse kundicotsera coipa canga,

3. Cifukwa ndazindikira macimo anga;Ndipo coipa canga ciri pamaso panga cikhalire:

4. Pa Inu, Inu nokha, ndinacimwa,Ndipo ndinacicita coipaco pamaso panu:Kuti mukhale wolungama pakulankhula Inu,Mukhalenso woyera pa kuweruza kwanu.

5. Onani, ndinabadwa m'mphulupulu:Ndipo mai wanga anandilandira m'zoipa.

6. Onani, Inu mukondwera ndi zoonadi m'malo a m'katimo;Ndipo m'malo a m'tseri mudzandidziwitsa nzeru.

7. Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera;Munditsuke ndipo ndidzakhala wa mbu woposa matalala.

8. Mundimvetse cimwemwe ndi kusekera:Kuti mafupawo munawatyola akondwere.

9. Muzibisire nkhope yanu zolakwa zanga,Ndipo mufafanize mphulupulu zanga zonse.

10. Mundilengere mtima woyera, Mulungu;Mukonze mzimu wokhazikika m'kati mwanga.

11. Musanditaye kundicotsa pamaso panu;Musandicotsere Mzimu wanu Woyera.

12. Mundibwezere cimwemwe ca cipulumutso canu;Ndipo mzimu wakulola undigwirizize.

13. Pomwepo ndidzalangiza ocimwa njira zanu;Ndipo olakwa adzabwera kwa Inu.

14. Mundilanditse ku mlandu wa mwazi, Mulungu,Ndinu Mulungu wa cipulumutso canga;Lilime langalidzakweza Nyimbo ya cilungamo canu.

15. Ambuye, tsegulani pa milomo yanga;Ndipo pakamwa panga padzalalikira ulemekezo wanu.

16. Pakuti simukondwera ndi nsembe, mwenzi nditapereka;Nsembe yopsereza simuikonda.

17. Nsembe za Mulungu ndizo mzimu wosweka;Inu, Mulungu, simudzaupeputsa mtima wosweka ndi wolapa.

18. Citirani Ziyoni cokoma monga mwa kukondwera kwanu;Mumange malinga a miyala a Yerusalemu.

19. Pamenepo mudzakondwera nazo nsembe zacilungamo,Ndi nsembe yopsereza ndi yopsereza yathunthu:Pamenepo adzaperekaNg'ombe pa guwa lanu la nsembe.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 51