8. Kucita cikondwero canu kundikonda, Mulungu wanga;Ndipo malamulo anu ali m'kati mwamtima mwanga.
9. Ndalalikira cilungamo mu msonkano waukuru;Onani, sindidzaletsa milomo yanga,Mudziwa ndinu Yehova.
10. Cilungamo canu sindinacibisa m'kati mwamtima mwanga;Cikhulupiriko canu ndi cipulumutso canu ndinacinena;Cifundo canu ndi coonadi canu sindinacibisira msonkhano waukuru.
11. Inu Yehova, simudzandikaniza nsoni zanu:Cifundo canu ndi coonadi canu zindisunge cisungire.
12. Pakuti zoipa zosawerengeka zandizinga,Zocimwa zanga zandipeza kotero kuti sindikhoza kupenya;Ziposa tsitsi la mutu wanga, ndipo wandicokera mtima.
13. Ndikupemphani, Yehova, ndilanditseni:Fulumirani kudzandithandiza, Yehova.
14. Acite manyazi nadodomeIwo akulondola moyo wanga kuti auononge:Abwerere m'mbuyo, nacite manyazi iwo okondwera kundicitira coipa.