1. Kuyembekeza ndayembekeza Yehova;Ndipo anandilola, namva kupfuula kwanga.
2. Ndipo anandikweza kunditurutsa m'dzenje la citayiko, ndi m'thope la pacithaphwi;Nandipondetsa pathanthwe, nakhazika mayendedwe anga.
3. Ndipo anapatsa Nyimbo yatsopano m'kamwa mwanga, cilemekezo ca kwa Mulungu wanga;Ambiri adzaciona, nadzaopa,Ndipo adzakhulupirira Yehova.
4. Wodala munthuyo wakuyesa Yehova wokhulupirika;Wosasamala odzikuza, ndi opatukira kubodza.
5. Inu, Yehova, Mulungu wanga, zodabwiza zanu mudazicita nzambiri,Ndipo zolingirira zanu za pa ife;Palibe wina wozifotokozera Inu;Ndikazisimba ndi kuzichula, Zindicurukira kuziwerenga.
6. Nsembe ndi copereka simukondwera nazo;Mwanditsegula makutu:Nsembe yopsereza ndi yamacimo simunapempha.
7. Pamenepo ndinati, Taonani, ndadza;M'buku mwalembedwa za Ine: