Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 17:1-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yehova, imvani cilungamo, mverani mpfuu wanga;Cherani khutu ku pemphero langa losaturuka m'milomo ya cinyengo,

2. Pankhope panu paturuke ciweruzo canga;Maso anu apenyerere zolunjika,

3. Mwayesera mtima wanga; mwandizonda usiku;Mwandisuntha, simupeza kanthu;Ndatsimikiza mtima kuti m'kamwa mwanga simudzalakwa.

4. Za macitidwe a anthu, ndaceniera ndi mau a milomo yanuNdingalowe njira za woononga.

5. M'mayendedwe anga ndasunga mabande anu,Mapazi anga sanaterereka.

6. Ine ndinakuitanani, pakuti mudzandiyankha, Mulungu:Cherani khutu lanu kwa ine, imvani mau anga.

7. Onetsani cifundo canu codabwiza, Inu wakupulumutsa okhulupirira InuKwa iwo akuwaukira ndi dzanja lanu lamanja.

8. Ndisungeni monga kamwana ka m'diso,Ndifungatireni mu mthunzi wa mapiko anu,

9. Kundilanditsa kwa oipa amene andipasula,Adani a pa moyo wanga amene andizinga.

10. Mafuta ao awatsekereza;M'kamwa mwao alankhula modzikuza.

11. Tsopano anatizinga m'mayendedwe athu:Apenyetsetsa m'maso kuti atigwetse pansi.

12. Afanana ndi mkango wofuna kumwetula,Ndi msona wa mkango wakukhala mobisalamo.

13. Ukani Yehova,Mumtsekereze, mumgwetse:Landitsani moyo wanga kwa woipa ndi lupanga lanu;

14. Kwa anthu, ndi dzanja lanu, Yehova,Kwa anthu a dziko lapansi pano amene colowa cao ciri m'moyo uno,Ndipo mimba yao muidzaza ndi cuma canu cobisika:Akhuta mtima ndi ana,Nasiyira ana amakanda zocuruka zao.

15. Koma ine ndidzapenyerera nkhope yanu m'cilungamo:Ndidzakhuta mtima ndi maonekedwe anu, pamene ndidzauka.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 17