Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 139:17-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Potero, Mulungu, ndiziyesa zolingalira zanu za mtengo wace ndithu!Mawerengedwe ace ndi ambirimbiri!

18. Ndikaziwerenga zicuruka koposa mcenga:Ndikauka ndikhalanso nanu.

19. Indedi, mudzaomba woipa, Mulungu:Ndipo amuna inu nkhumba mwazi, cokani kwa ine.

20. Popeza anena za Inu moipa,Ndi adani anu achula dzina lanu mwacabe.

21. Kodi sindidana nao iwo akudana ndi Inu, Yehova?Ndipo kodi sindimva nao cisoni iwo akuukira Inu?

22. Ndidana nao ndi udani weni weni:Ndiwayesa adani.

23. Mundisanthule, Mulungu, nimudziwe mtima wanga;Mundiyese nimudziwe zolingalira zanga.

24. Ndipo mupenye ngati ndiri nao mayendedwe oipa,Nimunditsogolere pa njira yosatha.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 139