Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 139:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo ndikati, Koma mdima undiphimbe,Ndi kuunika kondizinga kukhale usiku:

12. Ungakhale mdima sudetsa pamaso panu,Koma usiku uwala ngati usana:Mdima ukunga kuunika.

13. Pakuti Inu munalenga imso zanga;Munandiumba ndisanabadwe ine.

14. Ndikuyamikani cifukwa kuti cipangidwe canga ncoopsa ndi codabwiza;Nchito zanu nzodabwiza;Moyo wanga ucidziwa ici bwino ndithu.

15. Thupi langa silinabisikira Inu popangidwa ine mobisika,Poombedwa ine monga m'munsi mwace mwa dziko lapansi.

16. Ndisanaumbidwe ine maso anu anandipenya,Ziwalo zanga zonse zinalembedwa m'buku mwanu,Masiku akuti ziumbidwe, Pakalibe cimodzi ca izo.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 139