Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 103:9-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Sadzatsutsana nao nthawi zanse;Ndipo sadzasunga mkwiyo wace kosatha.

10. Sanaticitira monga mwa zolakwa zathu,Kapena kutibwezera monga mwa mphulupulu zathu.

11. Pakuti monga m'mwamba mutalikira ndi dziko lapansi,Motero cifundo cace cikulira iwo akumuopa Iye.

12. Monga kum'mawa kutanimpha ndi kumadzulo,Momwemo anatisiyanitsira kutali zolakwa zathu.

13. Monga atate acitira ana ace cifundo,Yehova acitira cifundo iwo akumuopa Iye.

14. Popeza adziwa mapangidwe athu;Akumbukila kuti ife ndife pfumbi.

15. Koma munthu, masiku ace akunga udzu;Aphuka monga duwa la kuthengo.

16. Pakuti mphepo ikapitapo pakhala palibe:Ndi malo ace salidziwanso.

17. Koma cifundo ca Yehova ndico coyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha kwa iwo akumuopa Iye,Ndi cilungamo cace kufikira kwa ana a ana;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 103