Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 103:14-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Popeza adziwa mapangidwe athu;Akumbukila kuti ife ndife pfumbi.

15. Koma munthu, masiku ace akunga udzu;Aphuka monga duwa la kuthengo.

16. Pakuti mphepo ikapitapo pakhala palibe:Ndi malo ace salidziwanso.

17. Koma cifundo ca Yehova ndico coyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha kwa iwo akumuopa Iye,Ndi cilungamo cace kufikira kwa ana a ana;

18. Kwa iwo akusunga cipangano cace,Ndi kwa iwo akukumbukila malangizo ace kuwacita.

19. Yehova anakhazika mpando wacifumu wace Kumwamba;Ndi ufumu wace ucita mphamvu ponsepo,

20. Lemekezani Yehova, inu angelo ace;A mphamvu zolimba, akucita mau ace,Akumvera liu la mau ace.

21. Lemekezani Yehova, inu makamu ace onse;Inu atumiki ace akucita comkondweretsa Iye,

22. Lemekezani Yehova, inu, nchito zace zonse,Ponse ponse pali ufumu wace:Lemekeza Yehova, moyo wanga iwe.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 103