Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 103:12-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Monga kum'mawa kutanimpha ndi kumadzulo,Momwemo anatisiyanitsira kutali zolakwa zathu.

13. Monga atate acitira ana ace cifundo,Yehova acitira cifundo iwo akumuopa Iye.

14. Popeza adziwa mapangidwe athu;Akumbukila kuti ife ndife pfumbi.

15. Koma munthu, masiku ace akunga udzu;Aphuka monga duwa la kuthengo.

16. Pakuti mphepo ikapitapo pakhala palibe:Ndi malo ace salidziwanso.

17. Koma cifundo ca Yehova ndico coyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha kwa iwo akumuopa Iye,Ndi cilungamo cace kufikira kwa ana a ana;

18. Kwa iwo akusunga cipangano cace,Ndi kwa iwo akukumbukila malangizo ace kuwacita.

19. Yehova anakhazika mpando wacifumu wace Kumwamba;Ndi ufumu wace ucita mphamvu ponsepo,

20. Lemekezani Yehova, inu angelo ace;A mphamvu zolimba, akucita mau ace,Akumvera liu la mau ace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 103