Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Maliro 1:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Gori la zolakwa zanga lamangidwa ndi dzanja lace;Zalukidwa, zakwera pakhosi panga; iye wakhumudwitsa mphamvuyanga;Ambuye wandipereka m'manja mwao, sindithai kuwalaka.

15. Ambuye wapepula ngwazi zanga zonse pakati panga;Waitanira msonkhano pa ine kuti uphwanye anyamata anga,Ambuye wapondereza namwaliyo, mwana wamkazi wa Ziyoni, monga mopondera mphesa.

16. Cifukwa ca zimenezi ndilira; diso langa, diso langatu likudza madzi:Pakuti wonditonthoza, wotsitsimutsa moyo wanga, anditarikira;Ana anga asungulumwa, pakuti adaniwo apambana.

17. Ziyoni atambasula manja ace, palibe wakumtonthoza;Yehova walamulira kuti omzungulira Yakobo akhale adani ace;Yerusalemu wasanduka cinthu conyansa pakati pao.

18. Yehova ali wolungama; pakuti ndapikisana ndi m'kamwa mwace:Mudtvetu, mitundu ya anthu nonsenu, nimuone cisoni canga;Anamwali ndi anyamata anga atha kulowa m'ndende.

Werengani mutu wathunthu Maliro 1