Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Maliro 1:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ha! mudziwo unadzala anthu, ukhalatu pa wokha!Ukunga mkazi wamasiye!Waukuruwo mwa amitundu, kalonga wamkazi m'madera a dzikoWasanduka wolamba!

2. Uliralira usiku; misozi yace iri pa masaya ace;Mwa onse amene anaukonda mulibe mmodzi wakuutonthoza:Mabwenzi ace onse aucitira ziwembu,Asanduka adani ace.

3. Yuda watengedwa ndende cifukwa ca msauko ndi ukapolo waukuru;Akhala mwa amitundu, sapeza popuma;Onse akumlondola anampeza pakati popsinjikiza.

4. M'njira za Ziyoni mulira posoweka akudzera msonkhano;Pa zipata zace zonse papasuka; ansembe ace onse ausa moyo;Anamwali ace asautsidwa; iye mwini namva zowawa.

Werengani mutu wathunthu Maliro 1