Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Malaki 3:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Mubwere nalo limodzi limodzi lonse la khumi, ku nyumba yosungiramo, kuti m'nyumba mwanga mukhale cakudya; ndipo mundiyese nako tsono, ati Yehova wa makamu, ngati sindikutsegulirani mazenera a kumwamba, ndi kukutsanulirani mdalitso wakuti adzasoweka malo akuulandira.

11. Ndipo ndidzadzudzula zolusa cifukwa ca inu, kuti zisakuonongereni zipatso za nthaka yanu; ngakhale mpesa wanu sudzayoyoka zipatso zace, zosaca m'munda, ati Yehova wa makamu.

12. Ndipo amitundu onse adzacha inu odala; pakuti mudzakhala dziko lokondweretsa, ati Yehova wa makamu.

13. Mau anu andilimbira, ati Yehova. Koma inu mukuti, Tanena motsutsana nanu ndi ciani?

14. Mwanena, Kutumikira Mulungu nkwa cabe; ndipo tapindulanji ndi kusunga udikiro wace, ndi kuyenda obvala zamaliro pamaso pa Yehova wa makamu?

Werengani mutu wathunthu Malaki 3