Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Malaki 1:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Pakuti kuyambira koturukira dzuwa kufikira kolowera kwace dzina langa lidzakhala lalikuru mwa amitundu; ndipo m'malo monse adzaperekera dzina langa cofukiza ndi copereka coona; pakuti dzina langa lidzakhala lalikuru mwa amitundu, ati Yehova wa makamu.

12. Koma inu muliipsa, pakunena inu, Gome la Yehova laipsidwa, ndi zipatso zace, cakudya cace, conyozeka.

13. Mukutinso, Taonani, ncolemetsa ici! ndipo mwacipeputsa, ati Yehova wa makamu; ndipo mwabwera nazo zofunkha, ndi zotsimphina, ndi zodwala; momwemo mubwera nayo nsembe; kodi ndiyenera kuilandira ku dzanja lanu? ati Yehova.

14. Koma wotembereredwa wonyengayo, wokhala nayo yaimuna m'gulu lace, nawinda, naphera Yehova nsembe cinthu cacirema; pakuti Ine ndine mfumu yaikuru, ati Yehova wa makamu; ndipo dzina langa ndi loopsa pakati pa amitundu.

Werengani mutu wathunthu Malaki 1