Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 9:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. ndi a nkhosa, ndi mcira wamafuta, ndi cophimba matumbo, ndi imso, ndi cokuta ca mphafa;

20. ndipo anaika mafuta pa ngangazo, natentha mafutawo pa guwa la nsembe.

21. Ndipo Aroni anaweyula ngangazo ndi mwendo wathako wa ku dzanja lamanja zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; monga iye anauza Mose.

22. Ndipo Aroni anakweza dzanja lace kulozera anthu, nawadalitsa; natsika kuja anapereka nsembe yaucimo, ndi nsembe yopsereza, ndi nsembe zoyamika.

23. Ndipo Mose ndi Aroni analowa ku cihema cokomanako, naturuka, nadalitsa anthu; ndipo ulemero wa Yehova unaonekera kwa anthu onse.

24. Ndipo unaturuka mota pamaso ya Yehova, nunyeketsa nsembe yopsereza ndi mafuta pa guwa la nsembe; ndipo pakuciona anthu onse anapfuula, nagwa nkhope zao pansi.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 9