Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 8:31-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Ndipo Mose anati kwa Aroni ndi kwa ana ace amuna, Phikani nyamayi pakhomo pa cihema cokomanako; ndipo muidyere komweko ndi mkate uli mu mtanga wa nsembe zodzaza manja, monga ndinauza, ndi kuti, Aroni ndi ana ace aidye.

32. Koma cotsalira ca nyama ndi mkate mucitenthe ndi moto.

33. Ndipo musaturuka pa khomo la cihema cokomanako masiku asanu ndi awiri, kufikira anakwanira masiku a kudzaza manja kwanu; pakuti adzaze manja anu masiku asanu ndi awiri.

34. Monga anacita lero lino, momwemo Yehova anauza kucita, kukucitirani cotetezera.

35. Ndipo mukhale pakhomo pa cihema cokomanako masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku, ndi kusunga cilangizo ca Yehova, kuti mungafe; pakuti anandiuza kotero.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 8