Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 6:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. ndipo wansembeyo amcitire comtetezera pamaso pa Yehova, ndipo adzakhululukidwa; kunena ziti zonse akazicita ndi kuparamula nazo.

8. Ndipo Yehova analankhula ndi Mose, nati,

9. Uza Aroni ndi ana ace, ndi kuti, Cilamulo ca nsembe yopsereza ndi ici: nsembe yopsereza izikhala pa nkhuni za pa guwa la nsembe usiku wonse kufikira m'mawa; ndipo mota wa pa guwa la nsembe uziyakabe pamenepo.

10. Ndipo wansembe abvale mwinjiro wace wabafuta, nabvale pathupi pace zobvala za pamiyendo zabafuta; naole phulusa, mota utanyeketsa nsembe yamoto pa guwa la nsembe, nalitaye m'mphepete mwa guwa la nsembe.

11. Pamenepo abvule zobvala zace, nabvale zobvala zina, nacotse phulusa kumka nalo kunja kwa cigono, kumalo koyera.

12. Ndipo mota wa pa guwa la nsembe uyakebe pamenepo, wosazima; wansembe ayatsepo nkhuni m'mawa ndi m'mawa; nakonzepo nsembe yopsereza, natenthepo mafuta a nsembe zoyamika.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 6