Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 6:27-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ali yense akakhudza nyama yace adzakhala wopatulika; ndipo akawaza mwazi wace wina pa cobvala ciri conse, utsuke cimene adauwazaco m'malo opatulika.

28. Ndipo mphika wadothi umene anaphikamo nyamayi auswe, koma ngati anaiphika mu mphika wamkuwa, atsuke uwu, nautsukuluze ndi madzi.

29. Amuna onse a mwa ansembe adyeko; ndiyo yopatulikitsa.

30. Koma asadye nsembe yaucimo iri yonse, imene amadza nao mwazi wace ku cihema cokomanako kutetezera nao m'malo opatulika; aitenthe ndi moto.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 6