12. inde ng'ombe yonse, kunja kwa cigono, kumka nayo kumalo koyera, kumene atayako mapulusa, naitenthe pankhuni ndi moto; aitenthe potayira mapulusa.
13. Ndipo khamu lonse la Israyeli likalakwa osati dala, ndipo cikabisika cinthuci pamaso pa msonkhano, litacita cina ca zinthu ziri zonse aziletsa Yehova, ndi kuparamula;
14. kukadziwika kucimwa adacimwako, pamenepo msonkhano uzibwera nayo ng'ombe yamphongo, ikhale nsembe yaucimo, ndipo udze nayo ku khomo la cihema cokomanako.
15. Ndipo akuru a khamulo aike manja ao pamutu pa ng'ombeyo, pamaso pa Yehova; naiphe ng'ombeyo pamaso pa Yehova.
16. Ndipo wansembe wodzozedwayo adze nao mwazi wina wa ng'ombeyo ku cihema cokomanako;
17. nabviike cala cace m'mwazi wa nsembewo, nauwaze kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova, cakuno ca nsaru yocinga.