Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 27:8-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Koma cuma cace cikapanda kufikira kuyesa kwako, amuike pamaso pa wansembe, kuti wansembeyo amuyese; ndipo wansembeyo amuyese, monga akhoza iye amene anawinda.

9. Ndipo cikakhala ca nyama imene anthu amabwera nayo ikhale copereka ca Yehova, zonse zotere munthu akazipereka kwa Yehova zikhale zopatulika.

10. Asaisinthe, yokoma m'malo mwa yoipa, kapena yoipa m'malo mwa yokoma; ndipo akasinthadi nyama m'malo mwa inzace, pamenepo iyo ndi yosinthikayo zikhale zopatulika.

11. Ndipo cikakhala ca nyama yodetsa, imene sabwera nayo ikhale copereka ca Yehova, aike nyamayi pamaso pa wansembe;

12. ndipo wansembeyo aiyese mtengo wace, ingakhale yokoma kapena yoipa; monga uiyesa wansembewe, momwemo.

13. Ndipo akaiombola ndithu, pamenepo aonjezepo limodzi la magawo asanu la mtengo wace.

14. Munthu akapatula nyumba yace ikhale yopatulika kwa Yehova, wansembe aziiyesa mtengo wace, ingakhale yokoma kapena yoipa; monga wansembeyo aiyesa, ikhale momwemo.

15. Ndipo iye wakuipatula akaombola nyumba yace, aonjezepo limodzi la magawo asanu la ndalama za kuyesa kwako, ndipo idzakhala yace.

16. Munthu akapatulirako Yehova munda wace wace, uziuyesa monga mwa mbeu zace zikakhala; homeri wa barie uuyese wa masekeli makumi asanu a siliva.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 27