Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 26:7-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Mudzapitikitsa adani anu, ndipo adzagwa pamaso panu ndi lupanga,

8. Asanu ainu adzapitikitsa zana limodzi, ndi zana limodzi la inu adzapitikitsa zikwi khumi; ndi adani anu adzagwa pamaso panu ndi lupanga.

9. Ndipo ndidzatembenukira kwa inu, ndi kukubalitsani, ndi kukucurukitsani; ndipo ndidzakhazika cipangano canga ndinapangana nanuco.

10. Ndipo mudzadya za sundwe wakale ndi kuturutsa zakale cifukwa ca zatsopano.

11. Ndidzamanga kacisi wanga pakati pa inu, ndipo moyo wanga sudzanyansidwa nanu.

12. Ndipo ndidzayendayenda pakati pa inu, ndi kukhala Mulungu wanu ndi inu mudzakhala anthu anga.

13. Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakuturutsani m'dziko la Aigupto, kuti musakhale akapolo ao; ndipo ndinatyola mitengo ya magoli anu, ndi kukuyendetsani coweramuka.

14. Koma mukapanda kundimvera Ine, osacita malamulo awa onse;

15. ndipo mukakaniza malemba anga, ndi moyo wanu ukanyansidwa nao maweruzo anga, kotero kuti simudzacita malamulo anga onse, koma kutyola cipangano canga;

16. ndidzacitira inu icinso; ndidzakuikirani zoopsa, nthendayoondetsayam'cifuwa ndi malungo, zakulanda maso ndi mphamvu, ndi kuzunza moyo; ndipo mudzabzala mbeu zanu cabe, pope za adani anu adzazidya.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 26