Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 25:6-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo sabata la dzikoli likhale kwa inu la cakudya; kwa iwe, ndi mnyamata wako, ndi mdzakazi wako, ndi wolembedwa nchito yako, ndi mlendo wako wakugonera kwanu;

7. ndi ng'ombe zako, ndi nyama ziri m'dziko lako; zipatso zace zonse zikhale cakudya cao.

8. Ndipo uziwerengera masabata a zaka asanu ndi awiri, zaka zisanu ndi ziwiri kasanu ndi kawiri; kotero kuti zaka za masabata a zaka asanu ndi awiri, zifikire zaka makumi anai kudza zisanu ndi zinai.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 25