Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 25:31-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Koma nyumba za m'midzi yopanda linga aziyese monga minda ya m'dziko; ziomboledwe, zituruke m'caka coliza lipenga.

32. Kunena za midzi ya Alevi, nyumba za m'midzi yao yao, Alevi akhoza kuziombola nthawi zonse.

33. Ndipo munthu akagula kwa Mlevi, nyumba yogulayo yokhala m'mudzi wace wace, ituruke m'caka coliza lipenga, popeza nyumba za m'midzi ya Alevi ndizo zao zao mwa ana a Israyeli.

34. Koma dambo la podyera pao siligulika; popeza ndilo lao lao kosatha.

35. Ndipo mbale wako akasaukira cuma, ndi dzanja lace lisowa; iwe uzimgwiriziza; akhale nawe monga mlendo wakugonera kwanu.

36. Usamambwezetsa phindu, kapena cioniezero; koma uope Mulungu wako; kuti mbale wako akhale nawe.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 25