Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 25:24-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Potero muzilola liomboledwe dziko lonse muli nalo.

25. Mbale wako akasaukira cuma, nakagulitsa cace cace, pamenepo mombolo wace, mbale wace weni weni azidza, naombole cimene mbale wace anagulitsaco.

26. Ndipo munthu akasowa mombolo, koma dzanja lace lacionetsa, nacipeza cofikira kuciombola;

27. pamenepo awerenge zaka za kugulitsa kwace, nabwezere wosulayo zotsalirapo, nabwerere iye ku dziko lace.

28. Koma dzanja lace likapanda kupeza zofikira za kumbwezera, pamenepo cogulitsaco cikhale m'dzanja lace la iye adacigulayo, kufikira caka coliza lipenga; koma caka coliza lipenga cituruke, nabwerere iye ku dziko lace.

29. Munthu akagulitsa nyumba yogonamo, m'mudzi wa m'linga, aiombole cisanathe caka coigulitsa; kufikira kutha caka akhoza kuombola.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 25