1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose m'phiri la Sinai, ndi kuti,
2. Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Mutakalowa m'dziko limene ndikupatsani, dzikoli lizisungira Yehova Sabata.
3. Zaka zisanu ndi cimodzi ubzale m'munda mwako, ndi zaka zisanu ndi cimodzi udzombole mphesa zako, ndi kuceka zipatso zace;
4. koma caka cacisanu ndi ciwiri cikhale sabata lakupumula la dziko, sabata la Yehova; usamabzala m'munda mwako, usamadzombola mipesa yako.
5. Zophuka zokha zofikira masika usamazichera, ndi mphesa za mipesa yako yosadzombola usaziceka; cikhale caka copumula dziko.
6. Ndipo sabata la dzikoli likhale kwa inu la cakudya; kwa iwe, ndi mnyamata wako, ndi mdzakazi wako, ndi wolembedwa nchito yako, ndi mlendo wako wakugonera kwanu;
7. ndi ng'ombe zako, ndi nyama ziri m'dziko lako; zipatso zace zonse zikhale cakudya cao.
8. Ndipo uziwerengera masabata a zaka asanu ndi awiri, zaka zisanu ndi ziwiri kasanu ndi kawiri; kotero kuti zaka za masabata a zaka asanu ndi awiri, zifikire zaka makumi anai kudza zisanu ndi zinai.
9. Pamenepo uzitumizira lipenga lomveka m'mwezi wacisanu ndi ciwiri, tsiku lakhumi la mweziwo; tsiku la citetezero mutumizire lipenga lifikire m'dziko lanu lonse.
10. Ndipo mucipatule caka ca makumi asanu, ndi kulalikira kwa onse okhala m'dzikomo kuti akhale aufulu; muciyese caka coliza lipenga; ndipo mubwerere munthu ali yense ku zace zace, ndipo mubwerere yense ku banja lace.
11. Muciyese caka ca makomi asanuco coliza lipenga, musamabzala, kapena kuceka zophuka zokha m'mwemo; kapenakuceka mphesa zace za mipesa yosadzombola.
12. Popeza ndico caka coliza lipenga; muciyese copatulika, mudye zipatso zace kunja kwa munda.
13. Caka coliza lipenga ici mubwerere nonse ku zace zace.