Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 23:8-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Koma mubwere nayo kwa Yehova nsembe yamoto masiku asanu ndi awiri; pa tsiku lacisanu ndi ciwiri pakhale msonkhano wopatulika; musamacita nchito ya masiku ena.

9. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

10. Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Mutakalowa m'dziko limene ndikupatsani, ndi kuceka dzinthu zace, pamenepo muzidza nao mtolo wa zipatso zoyamba za masika anu kwa wansembe;

11. ndipo iye aweyule mtolowo pamaso pa Yehova, ulandirikire inu, tsiku lotsata sabata wansembe aweyule.

12. Ndipo tsiku loweyula mtolowo, ukonze mwana wa nkhosa wopanda cirema, wa caka cimodzi, akhale nsembe yopsereza ya Yehova.

13. Ndipo nsembe yaufa yace ikhale awiri a magawo khumi a ufa wosalala wosanganiza ndi mafuta, ndiyo nsembe yamoto ya Yehova, icite pfungo lokoma; ndi nsembe yace yothira ikhale yavinyo, limodzi la magawo anai la hini.

14. Musamadya mkate, kapena tirigu wokazinga, kapena ngala zaziwisi, kufikira tsiku lomweli, kufikira mutadza naco copereka ca Mulungu wanu; ndilo lemba losatha mwa mibadwo yanu m'nyumba zanu zonse.

15. Ndipo mudziwerengere kuyambira tsiku lotsata Sabata, kuyambira tsikuli mudadza nao mtolo wa nsembe yoweyula; pakhale masabata asanu ndi awiri amphumphu;

16. muwerenge masiku makumi asanu kufikira tsiku lotsata sabata lacisanu ndi ciwiri; pamenepo mubwere nayo kwa Yehova nsembe ya ufa watsopano.

17. Muturuke nayo m'zinyumba zanu mikate iwiri ya nsembe yoweyula, ikhale ya awiri a magawo khumi a efa; ikhale ya ufa wosalala, yopanga ndi cotupitsa, zipatso zoyamba za Yehova.

18. Ndipo mubwere nao pamodzi ndi mikate, ana a nkhosa asanu ndi awiri, opanda cirema a caka cimodzi, ndi ng'ombe yamphongo imodzi, ndi nkhosa zamphongo ziwiri; zikhale nsembe yopsereza ya Yehova, pamodzi ndi nsembe yao yaufa, ndi nsembe zao zothira, ndizo nsembe yamoto ya pfungo lokoma la Yehova.

19. Mukonzenso mwana wa mbuzi mmodzi akhale nsembe yaucimo, ndi ana a nkhosa awiri a caka cimodzi akhale nsembe yoyamika.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 23