40. Ndipo tsiku loyambali mudzitengere nthambi za mitengo yokoma, nsomo za kanjedza, ndi nthambi za mitengo yobvalira, ndi misondodzi ya kumtsinje; ndipo mukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu masiku asanu ndi awiri.
41. Ndipo muwasunge madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri m'caka; ndilo lemba losatha mwa mibadwo yanu; musunge mwezi wacisanu ndi ciwiri.
42. Mukhale m'misasa masiku asanu ndi awiri; onse obadwa m'dziko mwa Israyeli akhale m'misasa;
43. kuti mibadwo yanu ikadziwe lruti ndinakhalitsa ana a Israyeli m'misasa, pamene ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
44. Ndipo Mose anafotokozera ana a Israyeli nyengo zoikika za Yehova.