Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 20:18-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Munthu akagona ndi mkazi ali mumsambo, nakambvula, anabvula kasupe wace, ndi iye mwini anabvula kasupe wa nthenda yace; awadule onse awiri pakati pa anthu a mtundu wao.

19. Usamabvula mbale wa mai wako, kapena mlongo wa atate wako; popeza anabvula abale ace; asenze mphulupulu yao.

20. Munthu akagona ndi mkazi wa mbale wa atate wace, nabvula mbale wa atate wace; asenze kucimwa kwao; adzafa osaona ana.

21. Munthu akatenga mkazi wa mbale wace, codetsa ici; wabvula mbale wace; adzakhala osaona ana.

22. Potero muzisunga malemba anga onse, ndi maweruzo anga onse, kuwacita; lingakusanzeni inu dziko limene ndipita nanuko, kuti mukhale m'mwemo.

23. Musamatsata miyambo ya mtundu umene neliucotsa pamaso panu; popeza anacita izi zonse, nelinalema nao.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 20