23. Ndipo mukadzalowa m'dzikomo, ndi kubzalamitengo yamitundumitundu ikhale ya cakudya, muziyese zipatso zao monga kusadulidwa kwao; zaka zitatu muziyese zosadulidwa; zisadyedwa.
24. Koma caka cacinai zipatso zace zonse zikhale zopatulika, za kumlemekeza nazo Yehova.
25. Caka cacisanu muzidya zipatso zace, kuti zobala zace zikucurukireni inu; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
26. Musamadya kanthu ndi mwazi wace; musamacita nyanga, kapena kuombeza ula.
27. Musamameta mduliro, kapena kusenga m'mphepete mwa ndebvu zanu,
28. Musamadziceka matupi anu cifukwa ca akufa, kapena kutema mpbini; Ine ndine Yehova.
29. Usamaipsa mwana wako wamkazi ndi kumcititsa cigololo; lingadzale ndi cigololo dzikoli, ndi kudzazidwa nazo zocititsa manyazi.
30. Muzisunga masabata anga, ndi kucitira ulemu malo anga opatulika; Ine ndine Yehova.
31. Musamatembenukira kwa obwebweta, kapena anyanga; musawafuna, ndi kudetsedwa nao; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
32. Pali aimvi uziwagwadira, nucitire ulemu munthu wokalamba; nuope Mulungu wako; lnendine Yehova.
33. Ndipo mlendo akagonera m'dziko mwanu, musamamsautsa.
34. Mlendo wakugonera kwa inu mumuyese pakati pa inu monga wa m'dziko momwemo; umkonde monga udzikonda wekha; popeza munali alendo m'dziko la Aigupto; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.