Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 19:1-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

2. Nena ndi khamu lonse la ana a Israyeli, nuti nao, Muzikhala oyera; pakuti ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndine woyera.

3. Ali yense aopemai wace, ndi atate wace; nimusunge masabata anga; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

4. Musamatembenukira mafano, kapena kudzipangira mulungu woyenga; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

5. Ndipo pamene muphera Yehova nsembe yoyamika, muiphere kuti mulandiridwe.

6. Tsiku lomwelo mwaipha, ndi m'mawa mwace muidye; ngati katsalirako kanthu tsiku lacitatu, muzikatentha ndi moto.

7. Akakadya konse tsiku tacitatu kali conyansa, kosabvomerezeka:

8. koma ali yense akudyako adzasenza mphulupulu yace, popeza waipsa copatulidwa ca Yehova; ndi munthuyo amsadze, kumcotsa kwa anthu a mtundu wace.

9. Pakukolola dzinthu za m'dziko mwanu, usamakololetsa m'mphepete mwa munda wako, nusamakunkha khunkha.

10. Usamakunkha khunkha la m'munda wako wamphesa, usamazitola zidagwazi za m'munda wako wamphesa; uzisiyire wosauka ndi mlendo; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

11. Musamaba, kapena kunyenga, kapena kunamizana.

12. Musamalumbira monama ndi kuchula dzina langa, ungaipse dzina la Mulungu wako; Ine ndine Yehova.

13. Usamasautsa mnansi wako, kapena kulanda zace; mphotho yace ya wolipidwa isakhale ndi iwe kufikira m'mawa.

14. Usamatemberera wogontha; usamaika cokhumudwitsa pamaso pa wosaona; koma uziopa Mulungu wako; Ine ndine Yehova.

15. Musamacita cisalungamo pakuwemza mlandu; usamabvomereza munthu wosauka, kapena kulemekeza munthu womveka; uweruze mlandu wa munthu mnzako molungama.

16. Usamayendayenda nusinjirira mwa anthu a mtundu wako; usamatsata mwazi wa mnansi wako; Ine ndine Yehova.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 19