Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 14:8-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo iye wakutiayeretsedwe atsuke zobvala zace, namete tsitsi lace lonse, nasambe madzi, nakhale woyera; ndipo atatero alowe kucigono, koma agone pa bwalo la hema wace masiku asanu ndi awiri.

9. Ndipo tsiku lacisanu ndi ciwiri kudzakhala kuti amete tsitsi lace lonse la pamutu pace, ndi ndebvu zace, ndi nsidze zace, inde amete tsitsi lace lonse; natsuke zobvala zace, nasambe thupi lace ndi madzi, nakhale woyera.

10. Ndipo tsiku lacisanu ndi citatu atenge ana a nkhosa awiri, amuna opanda cirema, ndi mwana wa nkhosa mmodzi wamkazi wa caka cimodzi wopanda cirema, ndi atatu a magawo khumi a ufa wosalala ukhale nsembe yaufa, wosanganiza ndi mafuta, ndi muyeso umodzi wa mafuta.

11. Ndipo wansembe amene amyeretsayo, amuike munthu uja wakuti ayeretsedwe, ndi zinthu zija, pamaso pa Yehova, pa khomo la cihema cokomanako;

12. ndipo wansembe atenge mwana wa nkhosa mmodzi wamwamuna, nabwere naye akhale nsembe yoparamula, pamodzi ndi muyeso uja wa mafuta, naziweyule nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.

13. Ndipo akaphere mwana wa nkhosa wamwamuna paja amapherapo nsembe yaucimo, ndi nsembe yopsereza, pa malo popatulika; pakuti monga nsembe yaucimo momwemo nsembe yoparamula, nja wansembe; ndiyo yopatulikitsa.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 14