Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 13:45-52 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

45. Ndipo azing'amba zobvala zace za wakhate ali ndi nthendayo, ndi tsitsi la pamutu pace lizikhala lomasuka, naphimbe iye mlomo wace wa m'mwamba, napfuule, Wodetsedwa, wodetsedwa!

46. Masiku onse nthenda ikali pa iye azikhala wodetsedwa; ali wodetsedwa, agone pa yekha pokhala pace pakhale kunja kwa cigono.

47. Ndiponso ngati nthenda yakhate iri pa cobvala caubweya, kapena cathonje;

48. ngakhale iri pamuyaro, kapena pamtsendero, cathonje, kapena caubweya, ngakhale iri pa cikopa, kapena pa cinthu ciri conse copanga ndi cikopa;

49. ngati nthenda iri yobiriwira, kapena yofiira pacobvala, kapena pacikopa, kapena pamuyaro, kapena pamtsendero, kapena pa cinthu ciri conse copangika ndi cikopa, ndiyo nthenda yakhate; aziionetsa kwa wansembe;

50. ndipo wansembe aone nthendayo, nabindikiritse ciija ca nthenda masiku asanu ndi awiri;

51. naone nthenda tsiku lacisanu ndi ciwiri; ngati nthenda yakula pacobvala, ngakhale pamuyaro, kapena pamtsendero, kapena pacikopa, ziri zonse zanchito zopangika ndi cikopa; nthendayo ndiyo khate lofukuta; ndico codetsedwa.

52. Ndipo atenthe cobvalaco ngakhale muyaro wace, ngakhale mtsendero wace, caubweya kapena cathonje, kapena ciri conse cacikopa ciri ndi khate, ndilo khate lofetsa; acitenrhe ndi mote.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 13