Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 10:18-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Taonani, sanalowa nao mwazi wace m'malo opatulika m'katimo; mukadaidyera ndithu m'malo opatulika, monga ndinakuuzani.

19. Ndipo Aroni analankhula ndi Mose, nati, Taonani, lero abwera nayo nsembe yao yaucimo ndi nsembe yao yopsereza pamaso pa Yehova; ndipo zandigwera zotere; ndikadadya nsembe yaucimo lero, kukadakomera kodi pamaso pa Yehova?

20. Pamene Mose adamva ici cidamkomera pamaso pace.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 10